AMUPHERANJI CHILIMA ? IMFA YOWAWA YA SAULOS CHILIMA
HTML-код
- Опубликовано: 11 июн 2024
- A CHILIMA AMWALIRA PA NGOZI YA NDEGE
Dziko la Malawi lili pa chisoni chachikulu pamene nzika zake zikulira kwambiri kamba ka ngozi ya ndege imene yatenga miyoyo ya anthu asanu ndi anayi (9) amene ndikuphatikizapo wachiwiri wa mtsogoleri wa dziko lino a Saulos Klaus Chilima. Ndegeyi imene inanyamula anthuwa inagwa dzulo pa 10 June 2024 ku dera lotchedwa Nthungwa mu nkhalango ya Chikangawa m’boma la Mzimba. Mtsogoleri wa dziko lino a Lazarus Chakwera ndi amene alengeza ndikuwuza mtundu wa a Malawi pazakumwalira kwa a Chilima ndi anthu ena amene anali nawo mu ndegeyo masana alero pa 11 June 2024. Mukuyankhula kwawo, a Chakwera amene amanveka ndikuwoneka kuti ali ndi chisoni chachikulu, apempha anthu mdziko muno akhale pa umodzi a bata pa nthawi yovuta ngati imeneyi.
A Chilima amapita ku Mzuzu kuchoka ku Lilongwe komwe amati akapitilira kupita m’boma la Nkhatabay kumene amayenera kukakhala nawo pa mwambo woyika mmanda a Ralph Kasambara amene anamwalira ku mapeto kwa sabatayi. Komatu za chisoni, nyengo ya chifunga inakakamiza ndege ya asilikali ankhondo adziko lino kuti ibwelere ku Lilongwe itakanika kutera pa bwalo la Mzuzu ndipo kuchoka apo, akulu akulu owona za ma ulendo a pandege ku Mzuzu ko sanathenso kuyankhula nayo ndegeyo.
To be aware is to be alive #MCP poly tricks #assassinations #RIP #vicePRESIDENT #saulosCHILIMA
We here bro
Mutu wa nkhaniwo ndizonwe mukuforokozazo zikusephana,and zoti achita kumupha ife tazidziwa kale through Limpopo FM Inu mwatsalira pati
Ilinde boza lenileni kodi amayendesa ndege anali chakwela koma munyasa anakonza nde chabwino poti inu mukuziwabwino mulindiumboni bwanji mutithandize mupite kupolisi mukawafotokozele venvenve wankhaniyi kuti amene apanga izizi amangidwe chifukwa or atakhala president amamangidwa bola umboniwanuwo please tithandizeni chilungamo chilibe mantha
Ndipo inu mmmm
Nkhani ndiyoti mcp yampha anthu 8 + vice president saulos chirima,enanu mutsutse musatsutse izi ndizomwe a Malawi akudziwa,CHIFUKWA ngozi ikachitika anthu ma foni amapezeka kena kotchedwa black box kamayenera kupezeka koma apo kanazulidwa anazula ndani konseko kufuna kubisa umboni kutenga ma phone a anthu akufao kufuna kubisa umboni, MCP boma lakupha lapha tsogolo la amalawi,musaikire KUMBUYO mimbulu
Awaaaaa
Hello Hanifa TV kodi simungapeze wina olankhura bho bho, kuti adzitipatsira uthenga?
Ine nnatchela nkhutu kuti ndimva zogwirizana ndi mutu wankhani koma ai palibe chikumvekapo apa mmmm
Nchifukwa adawa anthu ayamba kuwasiya chifukwa mutu wakhani ndi khani zimasiyana
Linthumbu ndi lomwe lamupha mkulu uyu NDIGWESE APM WAZIGWESA YEKHA LERO
Kod lnuso mkularata chani voice yosamveka fundo apa nkhani ndiyoti mcp yatipha lfe amalawi achinyamata 😭😭ngt boza chilima wanthu wk lmozi kumpha anthu 10 osalakwa chilima Ralph ndi nonse akupherani kumoz kawuseni mtendere tilibe mawu zawo zayera
Nkhani tayiwona, kale ife mcp yapha chilima ndipo simuzawonaso vote inu a galu
Inuyo simumatha
Ndipo zero
Ndiwe mbuzi
Ungonena zamisala ...ndipo usamalankhule ngat ukuvina
Ine ndimadabwa kwambiri kwathu kuno kumalawi kaya ndimaganizo awumphawi kaya umbuli anthu tikuchita kuwona kuti anthu amwalila pangozi koma umunva wina ati mwamuphelangi m'mbale wathu nde funso kumati wamupha ndani oyendesa ndegeyo kapena ndani nanga woyendesayo kapena kuti amene anakwelanawo ndegeyo anayikonda infayo kuti amwalile zina tikamayankhula tizikhala ndiwumunthu oyendesa sangalole kuti agwese ndege aphe achilima poziwa kuti naye amwalila osatheka ndani safuna moyo
Kodi black box ili kuti ya ndegeyo
Ndi imene ingathandize kuuza anthufe amene tikulephera kupeza mayankho eni eni chifukwa zomwe tikuuzidwa sidzikumveka bwino
I don't think atayipeza anga bwere poyera mmmm ,koma kuona zinthu za a chilima mmm abale koma dziko munthu ndi oopsa shame kodi ndegeyo imayendera madzi or mphepo mmmm munthu wandiopsa hey
Wachita kuphedwa kodi???
Rip
Basi anyama yayikuluwo akhale vp si apenze mtima agalu chabe chabe apa ndiye mwazinyera mkabudula ndiye mudzawina bwa popanda n'gwilizano poti mudawinila those zipani npaka 30 kulimbana ndi chipani chimozi Hedeee tidzaonesana 2025 bola otsazi Inshaallah 😁😁😁😁😁
😢😢😢😢
😢😢😢
Well done Hanifa..nkhani yopatsa chidwi..koma mutu wankhaniwutu mwalakwitsa..Mzimu wa vote yanga upitilize kuwunsa mu mtendere..😢😢
Chakwera ndiye wapha anthuwa Ife tamva kale. Inu munalikuti
Awa nawonso kungotichedwesapo apa mutu wankhani ndizimene akuyankhula tsizikugwiridzana
Fotseki😢😢😮
Mutu ndi nkhani zizifananako pls
Tikufuna bakili muluzi tv yiyankhulepo
Ndiwe mbuzi title ndi nkhani zikusiana
Zimu wachima uuse muntendere
Awaso nde achitsilu kwambili bwanj
Nthawi inoyo ungamasemphanitse mutu wankhani?
Simutha ndinu opepela kwambili
Voice yanuyo simveka bwino mupeze wina azikuyankhulilani
Mukuonae😂😂
Zaziiiiii
Mutu wa nkhani, utiuza zina inuso ndeee tive ziti??????
Awaaaaanso mmene amawelengela nkhani zawoo , eish,
😂
😂😂😂😂
i dont like the way you read eish its boring
Zachamba palibe chomwe ndva zazi kunena mokakamizidwa kuti unene ngat voice yako sikuwoneka ngati osamatiyamba dala zopusa
Mutu wa nkhani ukupita Ku Blantyre zimene mukufotokonza zikupita Ku Zomba.... Yankhulani Ngati mnyamata.... Title and story must be the same... Come on man!!!!
Kodi iwe yangulani mutu wankhani
Uyu ndiwamatha kwambiri is not a freedom fighter that'swhy Bakili Muluzi TV is a best ever. Most of his story mmmm 2/10
Apa ndi amupheranji? Kapena mbiri yake?
Hanifa utube ithe, siimatha kulondoloza nkhani komanso ili ndi anthu osatha kuwelenga bwino nkhani kkkkkkkkkkk, makamaka uyu akuwelenga panoyu akungowelenga ngati bembelezi kkkkkkkkkkk
Rubbish video u R talking of useless things instead of tackling the heading...wa bakili muluzi uja ndi dolo osati iwe kutiuza za obvious
😂😂😂😂