Official Opposition Ndi Enoch Chihana Ndi Peter Mutharika Basi - Blessing Chaima Lozalio
HTML-код
- Опубликовано: 8 окт 2024
- On Nyasa VoiceBox, Blessings Chaima Lozalio from the Defenders Group for Good Governance insists that in Malawi, AFORD and DPP, along with their leaders Enoch Chihana and Arthur Peter Mutharika, are the only official opposition parties.
Pa Nyasa Voicebox, Blessings Chaima Lozalio wa Defenders Group for Good Governance wanenetsa kuti ku Malawi, AFORD ndi DPP pamodzi ndi atsogoleri awo a Enoch Chihana ndi Arthur Peter Mutharika ndi okhawo otsutsa boma.
#malawi
DPP 🎉🎉🎉🎉
Aford inatha ilibe mulalo ndiye bola nakhumbwa
Next year sazakhalanso ku opposition anzakhala ma ruling
Kod fetrizer amakagulaso Ku pharmacy? Ndinamvapo kut chikangawa anagulapo fetrizer Ku pharmacy
Alliance yabwino ndi UTM UDF PDP AND PP tikufuna ulamuliro wina osati DPP kapena MCP ayi. TAYESA MAULAMULIRO AWO NDI OLEPHERA
Akugula zipani kulephela kugula chimanga kuika mma adimac Komanso feteleza koma zipani zikugulidwazo nzosaganiza ayi
Izi zikuza chifukwa cha kusavomeleza kwa zipani zina zosusa 'kulowa mungwilizano ndi DPP
Ngwilizano sakakamizana
Koma akulu akulu kuvotera pampandonso DPP ndi tchimo lalikulu losakhululukidwa kwa mulungu. Mmene amapangira mtagalala achina JOMO mu Limbe muja kumavula anthu avala makaka azipani zina osatitu mbendera ayi zovala zanthupi akuti uvula chifukwa kummwera ndi kwa DPP. DPP siimalemekeza mafumu ayi Anaivula mfumu Mponda ya ku Balaka.Ngakhale mafumu amene siali achi Lomwe akamapezeka pa misonkhano ya DPP ndikumauza kuti kuno kuli njala bwana ndimangowanvera chisoni mafumuwa. Kuona munthu akumuuzayo dera lakwawotu kumene masapota ake ambiri kunadutsa namondwe ngakhale nditsiku limodzi lomwe lotuluka akangowayendera osati kwapatsa kanthu ayi timadziwa kuti ndi owumira.Bola Joyce Banda ndi Bakili anatuluka pamodzi ndi Chakwera. DPP chipani cha ULUKHU chichititsana manyazi okhaokha monga mmene anamenyedwera mokofi A Brown Mpinganjira mu meeting ndi marafians amu DPP. MMalawi muno chiyambire cha democracy munamvapo apart from DPP kuti chipani china chake anyamata ake amenya akuluakulu achipani? Izi amazitha ndi a DPP okha basi. Mutati muonetsetse ambiri amene amatukwa za munsalu pa social media ndi amene amasapota DPP
Aford inapita ndi mwini wake Chakufwa, Enock akufunitsitsa atakhala nduna ya boma. Check his interview with Brian Banda after he left Tonse Alliance, now he wants to make alliance with DPP so that if they win may be he will be a minister. Shame on you.
Aford ilibe kolowera yangokakamizika kupita ku DPP . Aford ikutha pa 16 September 2025. Sali ndi MP mmodzi pa 17 September 2025 adzakhala ali pa zero. Aifunse UDF za DPP awauza siidziwa za democracy imafuna kumaliza zipani zaena. MCP palibe chipani achisosola ayi anthu onse akulowa ku MCP achita kuchotsedwa ku DPP. Anthunutu musaganize kuti MMalawi muno poti zinthu zabvuta ndi MCP ndiye kuti anthu onse adzavotera DPP apo ndiye mukuzinamiza anthutu ali ndizipani zomwe amazikonda. Azavotera zimenezo.
DPP no more.
Good boy
Andale anzeru amene akufuna kuti chipani chao chilimbe sangafune mgwitizano panopa ayi chidukwa ndichakuti mukapanga alliance chipani chimene chaimika president anthu amachivotera chimenecho chifukwa anthu ambiri ndi osazindikira siungauze kuti phungu muvotere wa Aford president muvotere wa DPP. Anthu amavotera chipani chaimika president cho.Ndiye kutha kwazipani kumakhala pamenepo. Ndi 50+1 kulibwino zipani ziime pazokha pazokha zipeze ma MP. Mgwirizano udzakhale mtsogolo.Pamgwirizano chipani chaching'onocho chimakhala ku receiving end or titi kunchira kapena titi kumapeto
MCP yoipa akufuna nite akuganiza bwànji azipani zinawo
Ndizoona zipani zinazi zakudwa
Mbuzi ya munthu dpp singawine. Udf ndi pp ali ndi ufulu kuyima paokha.
Mbudzi ndi iweyo means wang'ona iwe